Nyimbo 143
Kuwala M’dziko Lamdima
-
M’dzikoli mulitu mdima,
Anthu sakumvera.
Koma taona kuwala,
Ngati m’bandakucha.
(KOLASI)
Uthenga wa M’lungu,
Wawala ngati dzuwa
M’dziko lamdimali.
Ukupatsa anthu
Onse chiyembekezo
Mdima watha.
-
Tidzutse omwe agona,
Poti nthawi yatha.
Ndipo tiwalimbikitse,
Tiwapempherere.
(KOLASI)
Uthenga wa M’lungu,
Wawala ngati dzuwa
M’dziko lamdimali.
Ukupatsa anthu
Onse chiyembekezo
Mdima watha.
(Onaninso Yoh. 3:19; 8:12; Aroma 13:11, 12; 1 Pet. 2:9.)