Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Nyimbo 143

Kuwala M’dziko Lamdima

Kuwala M’dziko Lamdima

(2 Akorinto 4:6)

  1. M’dzikoli mulitu mdima,

    Anthu sakumvera.

    Koma taona kuwala,

    Ngati m’bandakucha.

    (KOLASI)

    Uthenga wa M’lungu,

    Wawala ngati dzuwa

    M’dziko lamdimali.

    Ukupatsa anthu

    Onse chiyembekezo

    Mdima watha.

  2. Tidzutse omwe agona,

    Poti nthawi yatha.

    Ndipo tiwalimbikitse,

    Tiwapempherere.

    (KOLASI)

    Uthenga wa M’lungu,

    Wawala ngati dzuwa

    M’dziko lamdimali.

    Ukupatsa anthu

    Onse chiyembekezo

    Mdima watha.