Nyimbo 138
Inu Ndinu Yehova
-
Mulungu woona
Wachilengedwe chonse
Mulungu wamuyaya
Ndinudi Yehova.
Ndifetu amwayi
Kukhala anthu anu
Tilalika za inu,
Ku mitundu yonse.
(KOLASI)
Yehova, Yehova,
M’lungu ndinu nokha
Kumwambako ndi padziko.
Palibenso wina
Ndinudi Wamphamvuyonse
Onsetu adziwe
Yehova, Yehova,
M’lungu wathu ndinu nokha.
-
Tingathe kukhala,
Chilichonse mwasankha.
Tigwire ntchito yanu
Ndinudi Yehova
Mwatipatsa dzina
Tikhale Mboni zanu
Uwu ndi mwayi wathu
Tikutamandani
(KOLASI)
Yehova, Yehova,
M’lungu ndinu nokha
Kumwambako ndi padziko.
Palibenso wina
Ndinudi Wamphamvuyonse
Onsetu adziwe
Yehova, Yehova,
M’lungu wathu ndinu nokha.
(Onaninso 2 Mbiri 6:14; Sal. 72:19; Yes. 42:8.)