Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Nyimbo 138

Inu Ndinu Yehova

Inu Ndinu Yehova

(Salimo 83:18)

  1. Mulungu woona

    Wachilengedwe chonse

    Mulungu wamuyaya

    Ndinudi Yehova.

    Ndifetu amwayi

    Kukhala anthu anu

    Tilalika za inu,

    Ku mitundu yonse.

    (KOLASI)

    Yehova, Yehova,

    M’lungu ndinu nokha

    Kumwambako ndi padziko.

    Palibenso wina

    Ndinudi Wamphamvuyonse

    Onsetu adziwe

    Yehova, Yehova,

    M’lungu wathu ndinu nokha.

  2. Tingathe kukhala,

    Chilichonse mwasankha.

    Tigwire ntchito yanu

    Ndinudi Yehova

    Mwatipatsa dzina

    Tikhale Mboni zanu

    Uwu ndi mwayi wathu

    Tikutamandani

    (KOLASI)

    Yehova, Yehova,

    M’lungu ndinu nokha

    Kumwambako ndi padziko.

    Palibenso wina

    Ndinudi Wamphamvuyonse

    Onsetu adziwe

    Yehova, Yehova,

    M’lungu wathu ndinu nokha.